Phungu wanyumba yamalamulo kudera la Kum’mwera- chakum’mawa Kwa mzinda wa Blantyre a Sameer Suleiman apambana pachisankho chachipululala chomwe chachitika kuderali lachiwiri.
A Suleiman apambana pachisankhochi ndi mavoti 458 pamene yemwe amapikisana nawo a Wild Ndipo apeza mavoti 17.
Izi zikutanthauza kuti a Suleiman ndi omwe adzaimire pampando waphungu wanyumba yamalamulo pachipani Cha DPP kudera la Chigumula-BCA -Club Banana pachisankhochi chapa 16 September Chaka chino.