by Kingsley Sowa
0 comments

Mtsogoleri wachipani cha Malawi congress Dr. Lazarus Mccarthy Chakwera avomereza kugonja pachisankho chomwe chinachitika pa 16 September chaka chino.

Dr. Chakwera avomereza kugonja kwawo pamene amayankhula ku mtundu wa a Malawi ku nyumba ya boma mumzinda wa Lilongwe masana a lachitatu.

Dr. Chakwera ati achita izi pofuna kulemekeza chifuniro cha a Malawi povotera Professor Arthur Peter Mutharika achipani cha Democratic Progressive-DPP ngati mtsogoleri wadziko lino pachisankhochi.

Iwo atinso achita izi ngati njira imodzi yolimbikitsira bata ndi mtendere pakati pa a Malawi zomwenso ndi ngodya za demokalase.

Komabe a Chakwera apempha bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la MEC kufotokozera bwino a Malawi ena mwa madandaulo omwe zipani zandale kuphatikizirapo chipani cha Malawi Congress zinapereka pa zotsatira zachisankho.

Pomaliza iwo ati ndi okonzeka kugwira ntchito limodzi ndi a Mutharika ndicholinga chopititsa patsogolo chitukuko cha dziko lino.

Bungwe loyendetsa chisankho la MEC likuyembekezera kulengeza zotsatira zachisankho cha mtsogoleri wadziko lino nthawi ya 2 koloko masanawu.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00