Home Politics A Enala Yesaya achipani cha MCP apambana pazisankho zachipulula za aphungu kudera la Blantyre-Chichiri-Misesa.

A Enala Yesaya achipani cha MCP apambana pazisankho zachipulula za aphungu kudera la Blantyre-Chichiri-Misesa.

by Kingsley Sowa
0 comments

Yemwe akuimila paudindo waphungu kudera Blantyre-Chichiri-Misesa muchipani cha Malawi congress-MCP Enala Yesaya wapambana pachisankho chachipulula chomwe chachitika lachitatu pasukulu ya pulaimale ya Kanjedza.

A Yesaya apambana pachisankhochi ndi mavoti 287 kugonjetsa a Charles Mwambyale omwe apeza mavoti 45.

Iwo ati ndiwokondwa ndi kupambanaku ponena kuti kukutanthauza chikhulupiliro chomwe anthu akuderali alinacho pokweza amayi paudindo.

A Yesaya alimbikitsa anthu akuderali kuti apitilire kukhala pambuyo pawo mpaka patsiku lachisankho pomwe ati ndi wodzipereka kutukula derali.

Kumbali yake wachiwiri kwa mkulu wa achinyamata muchipani cha MCP a Isaac Ramsey Khan anati chisankhochi chayenda bwino ndipo ayamikila anthu otsatira chipanichi potsatira ndondomeko za demokalase posankha munthu wamkazi paudindowu.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00