Malinga ndi wachiwiri kwa mneneri wa polisi ya Limbe Sub Inspector Sam Kadyole, thupi la bambo Tambala linapezedwa likulendewera kudenga la nyumba yawo madzulo a lachiwiri pa 17 June.
Sub Inspector Kadyole auza Eagle FM online kuti kafukufuku akadadali mkati pakadalipanno ofuna kupeza chomwe bamboyu wadziphera.
Iwo apempha mzika za dziko lino kumafunsila uphungu oyenera kunthambi ya Victim support unit yomwe imapezeka pa polisi iliyonse yomwe alinayo pafupi pamene akumana ndi mavuto osiyanasiyana m’malo mochotsa moyo wawo.
M’mawu ake mfumu Chipagala yati izi ndi zodandaulitsa kaamba koti akhala akulimbikitsa anthu awo kuti azitha kugawana ndi anzawo komanso atsogoleri amipingo zankhawa zomwe akukumana nazo pamoyo wawo wa tsiku ndi tsiku.