Home Uncategorized Polisi ya Limbe yati chiwelengero cha milandu chatsika ndi 15 % mutheka ya chaka chino.

Polisi ya Limbe yati chiwelengero cha milandu chatsika ndi 15 % mutheka ya chaka chino.

by Kingsley Sowa
0 comments

Polisi ya Limbe yati chiwelengero cha milandu yomwe anthu akhala akupalamula chatsika ndi 15 % mutheka ya chaka chino.

Malinga ndi wachiwiri kwa mneneri wa polisi ya Limbe Sub inspector Sam Kadyole, polisi yi yakwanitsa kuchepetsa chiwelengerochi pamene milandu yokwana 159 ndi yomwe polisiyi yalandira kuchokera mu January kufika June chaka chino kuyerekeza ndi milandu188 yomwe polisiyi inali italandira munyengo ngati yomweyi chaka chatha.

A Kadyole ati chiwelengerochi chatsika kutsatira ndondomeko zosiyanasiyana zomwe polisi yi inakhazikitsa pofuna kuthana ndi mchitidwe waumbava ndi umbanda kuderali.
Iwo anati mwa zina polisiyi yakhala ikugwira ntchito limodzi ndi atsogoleri akumadera komanso kudzalidwa kwa makanema achinsinsi mumsika wa Limbe zomwe zathandizira kuti ntchito yogwira anthu umbava ndi umbanda ikhale yosavuta.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00

Connection Information

To perform the requested action, WordPress needs to access your web server. Please enter your FTP credentials to proceed. If you do not remember your credentials, you should contact your web host.

Connection Type