Home Politics Phungu yemwe akuyimira kudela la Blantyre-Chichiri-Misesa walonjeza zitukuko kudelali akazapambana chisankho mwezi wa September

Phungu yemwe akuyimira kudela la Blantyre-Chichiri-Misesa walonjeza zitukuko kudelali akazapambana chisankho mwezi wa September

by Kingsley Sowa
0 comments

Yemwe akuimira pampando wa phungu wanyumba yamalamulo kudera la Blantyre-Chichiri-Misesa Themba Mkandawire wayamba ntchito yokambirana ndi mafumu pazina mwa zitukuko zomwe akufuna kuchita pamene chisankho chapa 16 September chikuwandikira.

A Mkandawire omwe anapambana pazisankho zachipulula posachedwapa mchipani cha Democratic Progressive-DPP ati cholinga cha mikumanoyi ndi kufuna kukhazikitsa ubale wabwino pakati pawo ndi mafumu omwe amayang’anira anthu akudera.

Iwo ati mikumanoyi ithandizira kupititsa patsogolo ntchito zachitukuko kuderali lomwe kwa nthawi yaitali lakhala lili lotsalira pankhani yachitukuko.

Zina mwa zitukuko zomwe a Mkandawire ati akufuna kuchita kuderali ndi kuphatikizirapo kupaka phula msewu wa Limbe-Manje, kubweretsa magetsi kudera ka mfumu Mtambo komanso ntchito yokuza chipatala cha Limbe.

Picture: Kingsley Sowa

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00

Connection Information

To perform the requested action, WordPress needs to access your web server. Please enter your FTP credentials to proceed. If you do not remember your credentials, you should contact your web host.

Connection Type