by Kingsley Sowa
0 comments

Mtsogoleri wachipani cha Malawi congress Dr. Lazarus Mccarthy Chakwera avomereza kugonja pachisankho chomwe chinachitika pa 16 September chaka chino.

Dr. Chakwera avomereza kugonja kwawo pamene amayankhula ku mtundu wa a Malawi ku nyumba ya boma mumzinda wa Lilongwe masana a lachitatu.

Dr. Chakwera ati achita izi pofuna kulemekeza chifuniro cha a Malawi povotera Professor Arthur Peter Mutharika achipani cha Democratic Progressive-DPP ngati mtsogoleri wadziko lino pachisankhochi.

Iwo atinso achita izi ngati njira imodzi yolimbikitsira bata ndi mtendere pakati pa a Malawi zomwenso ndi ngodya za demokalase.

Komabe a Chakwera apempha bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la MEC kufotokozera bwino a Malawi ena mwa madandaulo omwe zipani zandale kuphatikizirapo chipani cha Malawi Congress zinapereka pa zotsatira zachisankho.

Pomaliza iwo ati ndi okonzeka kugwira ntchito limodzi ndi a Mutharika ndicholinga chopititsa patsogolo chitukuko cha dziko lino.

Bungwe loyendetsa chisankho la MEC likuyembekezera kulengeza zotsatira zachisankho cha mtsogoleri wadziko lino nthawi ya 2 koloko masanawu.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00

Connection Information

To perform the requested action, WordPress needs to access your web server. Please enter your FTP credentials to proceed. If you do not remember your credentials, you should contact your web host.

Connection Type