Mtsogoleri wachipani cha Malawi congress Dr. Lazarus Mccarthy Chakwera avomereza kugonja pachisankho chomwe chinachitika pa 16 September chaka chino.
Dr. Chakwera avomereza kugonja kwawo pamene amayankhula ku mtundu wa a Malawi ku nyumba ya boma mumzinda wa Lilongwe masana a lachitatu.
Dr. Chakwera ati achita izi pofuna kulemekeza chifuniro cha a Malawi povotera Professor Arthur Peter Mutharika achipani cha Democratic Progressive-DPP ngati mtsogoleri wadziko lino pachisankhochi.
Iwo atinso achita izi ngati njira imodzi yolimbikitsira bata ndi mtendere pakati pa a Malawi zomwenso ndi ngodya za demokalase.
Komabe a Chakwera apempha bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la MEC kufotokozera bwino a Malawi ena mwa madandaulo omwe zipani zandale kuphatikizirapo chipani cha Malawi Congress zinapereka pa zotsatira zachisankho.
Pomaliza iwo ati ndi okonzeka kugwira ntchito limodzi ndi a Mutharika ndicholinga chopititsa patsogolo chitukuko cha dziko lino.
Bungwe loyendetsa chisankho la MEC likuyembekezera kulengeza zotsatira zachisankho cha mtsogoleri wadziko lino nthawi ya 2 koloko masanawu.