Home Crime Bambo wa zaka 62 wafa poziombera ndi mfuti mumzinda wa Blantyre.

Bambo wa zaka 62 wafa poziombera ndi mfuti mumzinda wa Blantyre.

by Kingsley Sowa
0 comments

Bambo wa zaka 62, Frank Kayuni wafa ataziombela ndi mfuti m’mawa wa lachiwiri pa 15 July pachipatala cha Mwaiwathu mumzinda wa Blantyre pomwe amalandira thandizo la mankhwala.

Malinga ndi malipoti mkazi wa bamboyu anamva kulira kwa komanso kukuwa kwa bambowa kuchokera kuchipinda ndipo atathamangila kuchipindachi iwo anapeza bambo yu ali chikomokere.

Mothandizana ndi akubanja, iwo anathamangira nawo kuchipatala bambowa komwe amwalira akulandira thandizo la mankhwala.

Thupi la malemuwa analitengera kuchipatala cha Queen Elizabeth Central komwe achipatala anatsimikiza kuti bambowa amwalira kamba ka bala lamfuti pachifuwa.

Padakali pano apolisi akufufuzabe chifukwa chomwe malemuwa achitira izi.

Malemu Frank Kayuni amachokera m’mudzi mwa Chizali kwa mfumu yaikulu Mwalambia m’boma la Chitipa.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00

Connection Information

To perform the requested action, WordPress needs to access your web server. Please enter your FTP credentials to proceed. If you do not remember your credentials, you should contact your web host.

Connection Type