by Kingsley Sowa
0 comments

Khansala wadera la Chigumula a Wild Ndipo omwe anagonja pachisankho chachipulula kwa a Sameer Suleiman pachipani cha Democratic progressive-DPP ati ayimila derali ngati phungu oyima payekha pachisankho chapa 16 September.

A Ndipo awuza Eagle FM Online kuti pakadalipano alimbikitsa zokonzekera zawo zofuna kuimila ngati phungu wadera la Chigumula-BCA-Club Banana.

Iwo ati chidwi choimila ngati phungu oyima payekha kuderali chadza kutsatira mavuto ochuluka omwe analipo panthawi yachisankho chachipululachi.

A Ndipo ati ndi odzipereka kugwira ntchito yotukula derali akadzapambana pachisankho chomwe chikuyembekezera kuchitika pa 16 September.

‘Poyambira ndili napo kale kaamba koti kufikira pakadalipano ndine khansala wadera la Chigumula ndipo chikhulupiliro ndili nacho kuti chimene Mulungu anandilembera chichitika basi’, anatero Ndipo.

Panthawi yachisankho chachipulula chomwe chinachitika mwezi wa April chaka chino mumzinda wa Blantyre a Ndipo anagonja atapeza mavoti 17 kwa omwe amapikisana nawo a Sameer Suleiman anapeza mavoti 458.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00

Connection Information

To perform the requested action, WordPress needs to access your web server. Please enter your FTP credentials to proceed. If you do not remember your credentials, you should contact your web host.

Connection Type